×

Surah Al-Bayyinah in Chichewa

Quran Chichewa ⮕ Surah Bayyinah

Translation of the Meanings of Surah Bayyinah in Chichewa - نيانجا

The Quran in Chichewa - Surah Bayyinah translated into Chichewa, Surah Al-Bayyinah in Chichewa. We provide accurate translation of Surah Bayyinah in Chichewa - نيانجا, Verses 8 - Surah Number 98 - Page 598.

بسم الله الرحمن الرحيم

لَمْ يَكُنِ الَّذِينَ كَفَرُوا مِنْ أَهْلِ الْكِتَابِ وَالْمُشْرِكِينَ مُنفَكِّينَ حَتَّىٰ تَأْتِيَهُمُ الْبَيِّنَةُ (1)
Iwo amene sakhulupirira a m’gulu la anthu a m’Buku ndi anthu opembedza mafano, sadzasiya kusakhulupilira mpaka pamene zizindikiro zooneka zitaperekedwa kwa iwo
رَسُولٌ مِّنَ اللَّهِ يَتْلُو صُحُفًا مُّطَهَّرَةً (2)
Mtumwi wochokera kwa Mulungu amene ali kuwerenga kuchokera pa Masamba oyera
فِيهَا كُتُبٌ قَيِّمَةٌ (3)
Amene ali ndi malamulo angwiro ndi omveka bwino ochokera kwa Mulungu
وَمَا تَفَرَّقَ الَّذِينَ أُوتُوا الْكِتَابَ إِلَّا مِن بَعْدِ مَا جَاءَتْهُمُ الْبَيِّنَةُ (4)
Ndipo anthu okhulupirira Buku sanayambe kugawikana pakati pawo mpaka pamene zizindikiro zooneka zidaperekedwa kwa iwo
وَمَا أُمِرُوا إِلَّا لِيَعْبُدُوا اللَّهَ مُخْلِصِينَ لَهُ الدِّينَ حُنَفَاءَ وَيُقِيمُوا الصَّلَاةَ وَيُؤْتُوا الزَّكَاةَ ۚ وَذَٰلِكَ دِينُ الْقَيِّمَةِ (5)
Ndipo Al-Zalzala 659 iwo sadalamulidwe koma kuti azipembedza Mulungu ndipo kuti asapembedze wina aliyense koma Iye yekha ndipo kuti adzipemphera pa nthawi yake ndi kupereka msonkho wothandiza anthu osauka. Ndipo chimenechi ndicho chipembedzo chabwino
إِنَّ الَّذِينَ كَفَرُوا مِنْ أَهْلِ الْكِتَابِ وَالْمُشْرِكِينَ فِي نَارِ جَهَنَّمَ خَالِدِينَ فِيهَا ۚ أُولَٰئِكَ هُمْ شَرُّ الْبَرِيَّةِ (6)
Ndithudi iwo amene sakhulupirira amene ali pakati pa anthu a m’Buku, ndi anthu opembedza mafano, adzakhala ku moto wa ku Gahena. Iwo ndiwo oipa zedi pa zolengedwa zonse
إِنَّ الَّذِينَ آمَنُوا وَعَمِلُوا الصَّالِحَاتِ أُولَٰئِكَ هُمْ خَيْرُ الْبَرِيَّةِ (7)
Ndithudi iwo amene atsatira chikhulupiriro choonadi ndipo amachita ntchito zabwino ndiwo olemekezeka pa zolengedwa zonse
جَزَاؤُهُمْ عِندَ رَبِّهِمْ جَنَّاتُ عَدْنٍ تَجْرِي مِن تَحْتِهَا الْأَنْهَارُ خَالِدِينَ فِيهَا أَبَدًا ۖ رَّضِيَ اللَّهُ عَنْهُمْ وَرَضُوا عَنْهُ ۚ ذَٰلِكَ لِمَنْ خَشِيَ رَبَّهُ (8)
Mphotho yawo imene ili ndi Ambuye wawo ndi kuwaika m’minda imene imathiriridwa ndi madzi ya m’mitsinje pansi pake, kumene adzakhalako nthawi zonse. Mulungu ndi wosangalala ndi iwo ndipo nawonso ndi osangalala ndi Iye. M’menemo ndi m’mene munthu oopa Mulungu adzalandirire mphotho yake
❮ Previous Next ❯

Surahs from Quran :

1- Fatiha2- Baqarah
3- Al Imran4- Nisa
5- Maidah6- Anam
7- Araf8- Anfal
9- Tawbah10- Yunus
11- Hud12- Yusuf
13- Raad14- Ibrahim
15- Hijr16- Nahl
17- Al Isra18- Kahf
19- Maryam20- TaHa
21- Anbiya22- Hajj
23- Muminun24- An Nur
25- Furqan26- Shuara
27- Naml28- Qasas
29- Ankabut30- Rum
31- Luqman32- Sajdah
33- Ahzab34- Saba
35- Fatir36- Yasin
37- Assaaffat38- Sad
39- Zumar40- Ghafir
41- Fussilat42- shura
43- Zukhruf44- Ad Dukhaan
45- Jathiyah46- Ahqaf
47- Muhammad48- Al Fath
49- Hujurat50- Qaf
51- zariyat52- Tur
53- Najm54- Al Qamar
55- Rahman56- Waqiah
57- Hadid58- Mujadilah
59- Al Hashr60- Mumtahina
61- Saff62- Jumuah
63- Munafiqun64- Taghabun
65- Talaq66- Tahrim
67- Mulk68- Qalam
69- Al-Haqqah70- Maarij
71- Nuh72- Jinn
73- Muzammil74- Muddathir
75- Qiyamah76- Insan
77- Mursalat78- An Naba
79- Naziat80- Abasa
81- Takwir82- Infitar
83- Mutaffifin84- Inshiqaq
85- Buruj86- Tariq
87- Al Ala88- Ghashiya
89- Fajr90- Al Balad
91- Shams92- Lail
93- Duha94- Sharh
95- Tin96- Al Alaq
97- Qadr98- Bayyinah
99- Zalzalah100- Adiyat
101- Qariah102- Takathur
103- Al Asr104- Humazah
105- Al Fil106- Quraysh
107- Maun108- Kawthar
109- Kafirun110- Nasr
111- Masad112- Ikhlas
113- Falaq114- An Nas