The Quran in Chichewa - Surah Humazah translated into Chichewa, Surah Al-Humazah in Chichewa. We provide accurate translation of Surah Humazah in Chichewa - نيانجا, Verses 9 - Surah Number 104 - Page 601.

| وَيْلٌ لِّكُلِّ هُمَزَةٍ لُّمَزَةٍ (1) Tsoka kwa aliyense amene amajeda ndi kuononga mbiri ya anzake |
| الَّذِي جَمَعَ مَالًا وَعَدَّدَهُ (2) Amene amasonkhanitsa chuma chake ndi kumachiwerenga |
| يَحْسَبُ أَنَّ مَالَهُ أَخْلَدَهُ (3) Iye amaganiza kuti chuma chake chidzamuchititsa iye kukhala ndi moyo wamuyaya |
| كَلَّا ۖ لَيُنبَذَنَّ فِي الْحُطَمَةِ (4) Iyayi! Ndithudi iye adzaponyedwa ku moto woononga |
| وَمَا أَدْرَاكَ مَا الْحُطَمَةُ (5) Kodi chidzakuuza kuti moto woononga ndi chiyani |
| نَارُ اللَّهِ الْمُوقَدَةُ (6) Ndi moto wa Mulungu umene Mwini wake anauyatsa |
| الَّتِي تَطَّلِعُ عَلَى الْأَفْئِدَةِ (7) Umene umafuka m’mitima ya anthu |
| إِنَّهَا عَلَيْهِم مُّؤْصَدَةٌ (8) Ndithudi udzawatsekereza mbali iliyonse |
| فِي عَمَدٍ مُّمَدَّدَةٍ (9) M’sanamila zoima |