×

Ndipo Ife tidalamula munthu kuti azichita zabwino kwa makolo ake. Amayi ake 46:15 Chichewa translation

Quran infoChichewaSurah Al-Ahqaf ⮕ (46:15) ayat 15 in Chichewa

46:15 Surah Al-Ahqaf ayat 15 in Chichewa (نيانجا)

Quran with Chichewa translation - Surah Al-Ahqaf ayat 15 - الأحقَاف - Page - Juz 26

﴿وَوَصَّيۡنَا ٱلۡإِنسَٰنَ بِوَٰلِدَيۡهِ إِحۡسَٰنًاۖ حَمَلَتۡهُ أُمُّهُۥ كُرۡهٗا وَوَضَعَتۡهُ كُرۡهٗاۖ وَحَمۡلُهُۥ وَفِصَٰلُهُۥ ثَلَٰثُونَ شَهۡرًاۚ حَتَّىٰٓ إِذَا بَلَغَ أَشُدَّهُۥ وَبَلَغَ أَرۡبَعِينَ سَنَةٗ قَالَ رَبِّ أَوۡزِعۡنِيٓ أَنۡ أَشۡكُرَ نِعۡمَتَكَ ٱلَّتِيٓ أَنۡعَمۡتَ عَلَيَّ وَعَلَىٰ وَٰلِدَيَّ وَأَنۡ أَعۡمَلَ صَٰلِحٗا تَرۡضَىٰهُ وَأَصۡلِحۡ لِي فِي ذُرِّيَّتِيٓۖ إِنِّي تُبۡتُ إِلَيۡكَ وَإِنِّي مِنَ ٱلۡمُسۡلِمِينَ ﴾
[الأحقَاف: 15]

Ndipo Ife tidalamula munthu kuti azichita zabwino kwa makolo ake. Amayi ake amavutika pomubereka ndi pomulera iye. Ndipo kuyambira pamene waberekedwa ndi pamene asiya kuyamwa ndi miyezi makumi atatu. Patapita nthawi iye amakula ndipo akakwanitsa zaka makumi anayi amati, “Ambuye wanga! Ndipatseni mphamvu ndi nzeru kuti ndikhale woyamika chifukwa cha chisoni chimene mwandionetsera ndi chimene mwaonetsera kwa makolo angakutindizichitazabwinozimenezidzakukondweretsani Inu. Ndipo chitireni zabwino zokhudza ana anga. Ndithudi ine ndiyang’ana kwa Inu polapa ndipo, ndithudi, ine ndine mmodzi wa anthu ogonjera.”

❮ Previous Next ❯

ترجمة: ووصينا الإنسان بوالديه إحسانا حملته أمه كرها ووضعته كرها وحمله وفصاله ثلاثون, باللغة نيانجا

﴿ووصينا الإنسان بوالديه إحسانا حملته أمه كرها ووضعته كرها وحمله وفصاله ثلاثون﴾ [الأحقَاف: 15]

Khaled Ibrahim Betala
“Ndipo tamulangiza munthu kuchitira zabwino makolo ake. Mayi wake adatenga pathupi pake mwamasautso; ndipo adam’bala mwamasautso. Kutenga pakati pake ndi kumsiitsa kuyamwa ndi miyezi makumi atatu. Kufikira atakula nsinkhu nkukwana zaka makumi anayi, (akakhala mwana wabwino) amanena: “E Mbuye wanga! Ndilimbikitseni kuthokoza mtendere Wanu umene mwandipatsa pamodzi ndi makolo anga, ndipo ndilimbitseni kuti ndizichita zabwino zimene (Inu) muziyanja ndipo ndikonzereni ndi kundilungamitsira ana anga. Ine ndatembenukira kwa Inu; ndiponso ine ndine m’modzi mwa ogonjera (Inu).”
❮ Previous Next ❯

Verse in more languages

Transliteration Bangla Bosnian German English Persian French Hindi Indonesian Kazakh Dutch Russian Spanish Turkish Urdu Uzbek