Quran with Chichewa translation - Surah An-Nisa’ ayat 171 - النِّسَاء - Page - Juz 6
﴿يَٰٓأَهۡلَ ٱلۡكِتَٰبِ لَا تَغۡلُواْ فِي دِينِكُمۡ وَلَا تَقُولُواْ عَلَى ٱللَّهِ إِلَّا ٱلۡحَقَّۚ إِنَّمَا ٱلۡمَسِيحُ عِيسَى ٱبۡنُ مَرۡيَمَ رَسُولُ ٱللَّهِ وَكَلِمَتُهُۥٓ أَلۡقَىٰهَآ إِلَىٰ مَرۡيَمَ وَرُوحٞ مِّنۡهُۖ فَـَٔامِنُواْ بِٱللَّهِ وَرُسُلِهِۦۖ وَلَا تَقُولُواْ ثَلَٰثَةٌۚ ٱنتَهُواْ خَيۡرٗا لَّكُمۡۚ إِنَّمَا ٱللَّهُ إِلَٰهٞ وَٰحِدٞۖ سُبۡحَٰنَهُۥٓ أَن يَكُونَ لَهُۥ وَلَدٞۘ لَّهُۥ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۗ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ وَكِيلٗا ﴾
[النِّسَاء: 171]
﴿ياأهل الكتاب لا تغلوا في دينكم ولا تقولوا على الله إلا الحق﴾ [النِّسَاء: 171]
Khaled Ibrahim Betala “E inu anthu a buku! Musamalumphe malire pa chipembedzo chanu. Ndipo musamamnenere Allah koma zowona (zokhazokha). Ndithu Mesiya Isa (Yesu) mwana wa Mariya, ndi mtumiki wa Allah (ndiponso ndi munthu wolengedwa) ndi liwu Lake lomwe adaliyika mwa Mariya ndiponso (ali) ndi mzimu (moyo) wochokera kwa Iye (Allah, monga mizimu ina yonse imachokera kwa Iye). Choncho Khulupirirani Allah ndi atumiki Ake. Musamanene: “Utatu wa Mulungu;” siyani, (zikhululupiliro za utatu wa Mulungu), kutero ndibwino kwa inu. Ndithudi, Allah ndi Mulungu m’modzi (basi). Ulemelero wake ngotukuka kutali ndi kukhala ndi mwana. Nzake zonse za kumwamba ndi pansi. Ndipo Allah ndiMtetezi Wokwanira |