×

Ndi pamene inu mudali tsidya lino la dambo ndi pamene anthu osakhulupirira 8:42 Chichewa translation

Quran infoChichewaSurah Al-Anfal ⮕ (8:42) ayat 42 in Chichewa

8:42 Surah Al-Anfal ayat 42 in Chichewa (نيانجا)

Quran with Chichewa translation - Surah Al-Anfal ayat 42 - الأنفَال - Page - Juz 10

﴿إِذۡ أَنتُم بِٱلۡعُدۡوَةِ ٱلدُّنۡيَا وَهُم بِٱلۡعُدۡوَةِ ٱلۡقُصۡوَىٰ وَٱلرَّكۡبُ أَسۡفَلَ مِنكُمۡۚ وَلَوۡ تَوَاعَدتُّمۡ لَٱخۡتَلَفۡتُمۡ فِي ٱلۡمِيعَٰدِ وَلَٰكِن لِّيَقۡضِيَ ٱللَّهُ أَمۡرٗا كَانَ مَفۡعُولٗا لِّيَهۡلِكَ مَنۡ هَلَكَ عَنۢ بَيِّنَةٖ وَيَحۡيَىٰ مَنۡ حَيَّ عَنۢ بَيِّنَةٖۗ وَإِنَّ ٱللَّهَ لَسَمِيعٌ عَلِيمٌ ﴾
[الأنفَال: 42]

Ndi pamene inu mudali tsidya lino la dambo ndi pamene anthu osakhulupirira adali tsidya ilo ndi magareta mmunsi mwanu. Ngakhale inu mukadagwirizana za malo okumana, inu mukadalephera kukwaniritsa chipanganocho koma Mulungu adafunitsitsa kuti akwaniritse zonse zimene adalamulira kuti aliyense amene adalembedwa kuti adzaonongeka, aonongeke pamene atalandira malangizo ooneka ndipo kuti iwo amene adalembedwa kuti asafe akhale ndi moyo atalandira malangizo ooneka. Ndithudi Mulungu ndi wakumva ndi wodziwa

❮ Previous Next ❯

ترجمة: إذ أنتم بالعدوة الدنيا وهم بالعدوة القصوى والركب أسفل منكم ولو تواعدتم, باللغة نيانجا

﴿إذ أنتم بالعدوة الدنيا وهم بالعدوة القصوى والركب أسفل منكم ولو تواعدتم﴾ [الأنفَال: 42]

Khaled Ibrahim Betala
“(Kumbukirani) pamene mudali mbali ya chigwa yoyandikira (mzinda wa Madina) pomwe iwo (ankhondo a Chikuraishi) adali mbali ya kutali ya tsidya lina (la chigwacho) pomwe aulendo amalonda adali cha kumunsi kwanu. Ngati mukadapangana nthawi yokumanirana (kuti mukumane nthawi yakutiyakuti), mukadasiyana posunga chipangano (chifukwa cha kuopa kuchuluka kwa adani anuwo). Koma (mwakumana mosayembekezera ndi ankhondo a adaniwo) kuti Allah akwaniritse chinthu chomwe nchofunika kuti chichitike, kuti awonongeke amene waonongeka (posankha kusakhulupirira) ndi umboni woonekera (umene adaukana kuutsata), ndi kuti akhale ndi moyo amene wakhala ndi moyo (amene watsata njira ya Chisilamu) ndi umboninso woonekera. Ndithudi Allah Ngwakumva zonse, Ngodziwa kwambiri
❮ Previous Next ❯

Verse in more languages

Transliteration Bangla Bosnian German English Persian French Hindi Indonesian Kazakh Dutch Russian Spanish Turkish Urdu Uzbek