×

Ndipo pamene iye adamva zokamba zawo, adawatumizira uthenga owaitana ndi kuwakonzera chakudya 12:31 Chichewa translation

Quran infoChichewaSurah Yusuf ⮕ (12:31) ayat 31 in Chichewa

12:31 Surah Yusuf ayat 31 in Chichewa (نيانجا)

Quran with Chichewa translation - Surah Yusuf ayat 31 - يُوسُف - Page - Juz 12

﴿فَلَمَّا سَمِعَتۡ بِمَكۡرِهِنَّ أَرۡسَلَتۡ إِلَيۡهِنَّ وَأَعۡتَدَتۡ لَهُنَّ مُتَّكَـٔٗا وَءَاتَتۡ كُلَّ وَٰحِدَةٖ مِّنۡهُنَّ سِكِّينٗا وَقَالَتِ ٱخۡرُجۡ عَلَيۡهِنَّۖ فَلَمَّا رَأَيۡنَهُۥٓ أَكۡبَرۡنَهُۥ وَقَطَّعۡنَ أَيۡدِيَهُنَّ وَقُلۡنَ حَٰشَ لِلَّهِ مَا هَٰذَا بَشَرًا إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا مَلَكٞ كَرِيمٞ ﴾
[يُوسُف: 31]

Ndipo pamene iye adamva zokamba zawo, adawatumizira uthenga owaitana ndi kuwakonzera chakudya ndipo kwa aliyense, adamupatsa mpeni wodyera. Ndipo adati kwa Yosefe, “Tulukira kumene kuli iwo.” Ndipo pamene iwo adamuona iye, onse adamulemekeza ndipo adadzicheka manja awo. Ndipo iwo adati, “Mulungu ayeretsedwe! Uyu si munthu ayi koma mngelo wolemekezeka.”

❮ Previous Next ❯

ترجمة: فلما سمعت بمكرهن أرسلت إليهن وأعتدت لهن متكأ وآتت كل واحدة منهن, باللغة نيانجا

﴿فلما سمعت بمكرهن أرسلت إليهن وأعتدت لهن متكأ وآتت كل واحدة منهن﴾ [يُوسُف: 31]

Khaled Ibrahim Betala
“Ndipo (mkazi wa nduna) pamene adamva kunyogodola kwawo, adawaitana (kuti adzaone kukongola kwa Yûsuf kuti adziwe kuti yemwe wathedwa nzeru polakalaka Yûsuf ngosayenera kudzudzulidwa). Ndipo adawakonzera phwando ndikupatsa aliyense wa iwo mpeni; kenaka adamuuza (Yûsuf): “Tuluka ndi kubwera pamaso pa iwo.” Choncho pamene (akazi aja) adamuona, adaona kuti nchinthu chachikulu zedi ndipo adadzicheka manja awo (ndi mipeni ija. Sadazindikire kuti akudzicheka chifukwa cha chidwi ndi kukongola kwa Yûsuf), ndipo adati: “Hasha Lillah! (tikudzitchinjiriza kwa Allah) uyu simunthu, uyu sichina koma ndi mngelo wolemekezeka.”
❮ Previous Next ❯

Verse in more languages

Transliteration Bangla Bosnian German English Persian French Hindi Indonesian Kazakh Dutch Russian Spanish Turkish Urdu Uzbek