×

Mulungu walonjeza ena a inu amene akhulupirira ndipo amachita ntchito zabwino kuti 24:55 Chichewa translation

Quran infoChichewaSurah An-Nur ⮕ (24:55) ayat 55 in Chichewa

24:55 Surah An-Nur ayat 55 in Chichewa (نيانجا)

Quran with Chichewa translation - Surah An-Nur ayat 55 - النور - Page - Juz 18

﴿وَعَدَ ٱللَّهُ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ مِنكُمۡ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ لَيَسۡتَخۡلِفَنَّهُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ كَمَا ٱسۡتَخۡلَفَ ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِهِمۡ وَلَيُمَكِّنَنَّ لَهُمۡ دِينَهُمُ ٱلَّذِي ٱرۡتَضَىٰ لَهُمۡ وَلَيُبَدِّلَنَّهُم مِّنۢ بَعۡدِ خَوۡفِهِمۡ أَمۡنٗاۚ يَعۡبُدُونَنِي لَا يُشۡرِكُونَ بِي شَيۡـٔٗاۚ وَمَن كَفَرَ بَعۡدَ ذَٰلِكَ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡفَٰسِقُونَ ﴾
[النور: 55]

Mulungu walonjeza ena a inu amene akhulupirira ndipo amachita ntchito zabwino kuti adzawasandutsa kukhala olowa m’malo padziko monga momwe adasandutsira anthu amene adalipo kale iwo asanadze. Ndipo Iye adzawapatsa mphamvu yoyendetsa chipembedzo chawo chimene adawasankhira. Ndithudi Iye adzawapatsa m’malo mwake chitetezo chokwana atawachokera mantha ngati iwo andipembedza Ine ndipo sandiphatikiza ndi china chilichonse. Ndipo onse amene sakhulupirira atamva izi ndi ochimwa

❮ Previous Next ❯

ترجمة: وعد الله الذين آمنوا منكم وعملوا الصالحات ليستخلفنهم في الأرض كما استخلف, باللغة نيانجا

﴿وعد الله الذين آمنوا منكم وعملوا الصالحات ليستخلفنهم في الأرض كما استخلف﴾ [النور: 55]

Khaled Ibrahim Betala
“Allah walonjeza mwa inu amene akhulupirira ndikuchita ntchito yabwino kuti ndithu awathandiza kukhala oyang’anira pa dziko monga momwe adawachitira amene adalipo kale kukhala oyang’anira; ndipo ndithu awalimbikitsira chipembedzo chawo chimene wawayanja nacho; ndipo awachotsera mantha awo kukhala opanda mantha.” Akhale akundilambira Ine, osandiphatikiza ndi chilichonse. Ndipo amene asiye kukhulupirira pambuyo pa zimenezi, iwo ngakuswa malamulo
❮ Previous Next ❯

Verse in more languages

Transliteration Bangla Bosnian German English Persian French Hindi Indonesian Kazakh Dutch Russian Spanish Turkish Urdu Uzbek