×

Oh inu anthu okhulupirira! Musaphe nyama za m’thengo pamene mutavala zobvala za 5:95 Chichewa translation

Quran infoChichewaSurah Al-Ma’idah ⮕ (5:95) ayat 95 in Chichewa

5:95 Surah Al-Ma’idah ayat 95 in Chichewa (نيانجا)

Quran with Chichewa translation - Surah Al-Ma’idah ayat 95 - المَائدة - Page - Juz 7

﴿يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَقۡتُلُواْ ٱلصَّيۡدَ وَأَنتُمۡ حُرُمٞۚ وَمَن قَتَلَهُۥ مِنكُم مُّتَعَمِّدٗا فَجَزَآءٞ مِّثۡلُ مَا قَتَلَ مِنَ ٱلنَّعَمِ يَحۡكُمُ بِهِۦ ذَوَا عَدۡلٖ مِّنكُمۡ هَدۡيَۢا بَٰلِغَ ٱلۡكَعۡبَةِ أَوۡ كَفَّٰرَةٞ طَعَامُ مَسَٰكِينَ أَوۡ عَدۡلُ ذَٰلِكَ صِيَامٗا لِّيَذُوقَ وَبَالَ أَمۡرِهِۦۗ عَفَا ٱللَّهُ عَمَّا سَلَفَۚ وَمَنۡ عَادَ فَيَنتَقِمُ ٱللَّهُ مِنۡهُۚ وَٱللَّهُ عَزِيزٞ ذُو ٱنتِقَامٍ ﴾
[المَائدة: 95]

Oh inu anthu okhulupirira! Musaphe nyama za m’thengo pamene mutavala zobvala za Hajji kapena Umra. Yense wa inu amene apha nyama mwadala, adzapereka, ngati dipo lofika ku Kaaba, nyama yoweta yofanana ndi imene iye wapha, imene idzatsimikizidwa ndi anthu awiri olungama amene ali pakati panu kapena m’malo mwake adzadyetsa anthu osauka kapena kusala kuti alawe kuipa kwa ntchito zake. Mulungu wakhululukira zonse za m’mbuyo koma ngati wina abwerera ku uchimo, Mulungu adzamulanga kwambiri. Mulungu ndi wamphamvu ndipo ndi mwini kubwezera

❮ Previous Next ❯

ترجمة: ياأيها الذين آمنوا لا تقتلوا الصيد وأنتم حرم ومن قتله منكم متعمدا, باللغة نيانجا

﴿ياأيها الذين آمنوا لا تقتلوا الصيد وأنتم حرم ومن قتله منكم متعمدا﴾ [المَائدة: 95]

Khaled Ibrahim Betala
“E inu amene mwakhulupirira! Musaphe nyama ya mtchire pomwe inu muli m’mapemphero a Hajj kapena Umrah. Ndipo mwa inu amene angaphe mwadala nyama ya mtchireyo, dipo (lake likhale kuzinga) yofanana ndi yomwe waphayo, mu mtundu wa nyama zowetedwa, (monga mmene) angaweruzire olungama awiri a mwa inu, kukhala nsembe yoperekedwa ku Ka’aba (kuti ikazingidwe kumeneko ndi kuwagawira osauka); kapena alipe dipo la chakudya kudyetsa masikini; kapena m’malo mwake asale kuti alawe kupweteka kwa chinthu chakecho. Ndipo Allah afafaniza zomwe zidapita kale. Koma amene achitenso, Allah amukhaulitsa ndi chilango chochokera kwa Iye. Ndipo Allah Ngwamphamvu zoposa, Wokhaulitsa koopsa
❮ Previous Next ❯

Verse in more languages

Transliteration Bangla Bosnian German English Persian French Hindi Indonesian Kazakh Dutch Russian Spanish Turkish Urdu Uzbek