×

Mulungu wakulamulirani motere pankhani za ana anu: Mwana wa mwamuma adzalandira magawo 4:11 Chichewa translation

Quran infoChichewaSurah An-Nisa’ ⮕ (4:11) ayat 11 in Chichewa

4:11 Surah An-Nisa’ ayat 11 in Chichewa (نيانجا)

Quran with Chichewa translation - Surah An-Nisa’ ayat 11 - النِّسَاء - Page - Juz 4

﴿يُوصِيكُمُ ٱللَّهُ فِيٓ أَوۡلَٰدِكُمۡۖ لِلذَّكَرِ مِثۡلُ حَظِّ ٱلۡأُنثَيَيۡنِۚ فَإِن كُنَّ نِسَآءٗ فَوۡقَ ٱثۡنَتَيۡنِ فَلَهُنَّ ثُلُثَا مَا تَرَكَۖ وَإِن كَانَتۡ وَٰحِدَةٗ فَلَهَا ٱلنِّصۡفُۚ وَلِأَبَوَيۡهِ لِكُلِّ وَٰحِدٖ مِّنۡهُمَا ٱلسُّدُسُ مِمَّا تَرَكَ إِن كَانَ لَهُۥ وَلَدٞۚ فَإِن لَّمۡ يَكُن لَّهُۥ وَلَدٞ وَوَرِثَهُۥٓ أَبَوَاهُ فَلِأُمِّهِ ٱلثُّلُثُۚ فَإِن كَانَ لَهُۥٓ إِخۡوَةٞ فَلِأُمِّهِ ٱلسُّدُسُۚ مِنۢ بَعۡدِ وَصِيَّةٖ يُوصِي بِهَآ أَوۡ دَيۡنٍۗ ءَابَآؤُكُمۡ وَأَبۡنَآؤُكُمۡ لَا تَدۡرُونَ أَيُّهُمۡ أَقۡرَبُ لَكُمۡ نَفۡعٗاۚ فَرِيضَةٗ مِّنَ ٱللَّهِۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلِيمًا حَكِيمٗا ﴾
[النِّسَاء: 11]

Mulungu wakulamulirani motere pankhani za ana anu: Mwana wa mwamuma adzalandira magawo awiri kuposa mwana wa mkazi. Ndipo ngati ana a akazi apitirira awiri, iwo adzalandira magawo awiri pa magawo atatu a katundu wosiyidwa koma ngati alipo mwana mmodzi yekha wamkazi, adzalandila theka ndipo makolo ake awiri, aliyense mwa iwo adzalandira gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi – muzimene adasiya malemuyo ngati malemuyo ali ndi mwana. Koma ngati alibe mwana ndipo makolo ake ndiwo amene ayenera kulandira katundu wake, amayi ake adzalandira gawo limodzi la magawo atatu. Ngati iye ali ndi abale ake, amayi ake adzalandira gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi atatha kukwaniritsa lonjezo la malemu ndiponso kubweza ngongole. Inu simudziwa kuti pakati pa makolo anu ndi ana anu amene ali wa phindu ndi inu. Ili ndi lamulo la Mulungu. Ndithudi Mulungu ndi wanzeru ndi wodziwa chilichonse

❮ Previous Next ❯

ترجمة: يوصيكم الله في أولادكم للذكر مثل حظ الأنثيين فإن كن نساء فوق, باللغة نيانجا

﴿يوصيكم الله في أولادكم للذكر مثل حظ الأنثيين فإن كن نساء فوق﴾ [النِّسَاء: 11]

Khaled Ibrahim Betala
“Allah akukulamulani za ana anu achimuna apate gawo lolingana ndi gawo la akazi awiri. Ngati akaziwo ali (opitilira) awiri, ndiye kuti adzalandira zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu (/3) za (chumacho) chimene wasiya (womwalira), ngati mwana wamkazi ndi mmodzi, apatsidwe gawo limodzi mwa magawo awiri (1/2), naonso makolo ake awiri aliyense wa iwo alandile gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (1/6) achuma chosiidwacho, ngati (womwalirayo) wasiya mwana (kapena mdzukulu). Koma ngati sadasiye mwana, ndipo makolo ake awiri ndiwo awasiira, ndiye kuti mayi wake alandire gawo limodzi mwamagawo atatu (1/3) achumacho, (ndipo bambo alandire 2/3). Ngati wakufayo wasiya abale, ndiye kuti mayi wake apeza gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (1/6) achumacho. (Kugawa chumaku kuchitike) atachotsapo chimene iye adalamulira kuti adzachipereke kwakutikwakuti, kapena kulipira ngongole (zake). Atate anu ndi ana anu, simudziwa inu kuti ndani mwa iwo amene ali ndi chithandizo chapafupi kwa inu. Amenewa ndi malamulo omwe akhazikitsidwa ndi Allah. Ndithudi, Allah ngodziwa kwambiri, Ngwanzeru zakuya
❮ Previous Next ❯

Verse in more languages

Transliteration Bangla Bosnian German English Persian French Hindi Indonesian Kazakh Dutch Russian Spanish Turkish Urdu Uzbek