×

Inu mudzalandira theka la chuma chimene akazi anu adasiya, ngati iwo alibe 4:12 Chichewa translation

Quran infoChichewaSurah An-Nisa’ ⮕ (4:12) ayat 12 in Chichewa

4:12 Surah An-Nisa’ ayat 12 in Chichewa (نيانجا)

Quran with Chichewa translation - Surah An-Nisa’ ayat 12 - النِّسَاء - Page - Juz 4

﴿۞ وَلَكُمۡ نِصۡفُ مَا تَرَكَ أَزۡوَٰجُكُمۡ إِن لَّمۡ يَكُن لَّهُنَّ وَلَدٞۚ فَإِن كَانَ لَهُنَّ وَلَدٞ فَلَكُمُ ٱلرُّبُعُ مِمَّا تَرَكۡنَۚ مِنۢ بَعۡدِ وَصِيَّةٖ يُوصِينَ بِهَآ أَوۡ دَيۡنٖۚ وَلَهُنَّ ٱلرُّبُعُ مِمَّا تَرَكۡتُمۡ إِن لَّمۡ يَكُن لَّكُمۡ وَلَدٞۚ فَإِن كَانَ لَكُمۡ وَلَدٞ فَلَهُنَّ ٱلثُّمُنُ مِمَّا تَرَكۡتُمۚ مِّنۢ بَعۡدِ وَصِيَّةٖ تُوصُونَ بِهَآ أَوۡ دَيۡنٖۗ وَإِن كَانَ رَجُلٞ يُورَثُ كَلَٰلَةً أَوِ ٱمۡرَأَةٞ وَلَهُۥٓ أَخٌ أَوۡ أُخۡتٞ فَلِكُلِّ وَٰحِدٖ مِّنۡهُمَا ٱلسُّدُسُۚ فَإِن كَانُوٓاْ أَكۡثَرَ مِن ذَٰلِكَ فَهُمۡ شُرَكَآءُ فِي ٱلثُّلُثِۚ مِنۢ بَعۡدِ وَصِيَّةٖ يُوصَىٰ بِهَآ أَوۡ دَيۡنٍ غَيۡرَ مُضَآرّٖۚ وَصِيَّةٗ مِّنَ ٱللَّهِۗ وَٱللَّهُ عَلِيمٌ حَلِيمٞ ﴾
[النِّسَاء: 12]

Inu mudzalandira theka la chuma chimene akazi anu adasiya, ngati iwo alibe mwana. Ngati ali ndi mwana, inu mudzalandira gawo limodzi la magawo anayi la zimene mkaziyo wasiya pambuyo popereka zimene analonjeza ndi kubwezera ngongole. Nawo akazi anu adzapeza gawo limodzi m’magawo anayi muzimene mwasiya ngati mulibe mwana. Koma ngati muli ndi mwana, iwo, akaziwo, adzapeza gawo limodzi la magawo asanu ndi atatu a zimene mwasiya, pambuyo popereka zimene mudalonjeza ndi kubwezera ngongole. Ngati mwamuna kapena mkazi ndi yemwe wasiya katundu ndipo alibe mwana kapena mdzukulu, koma ali ndi mchimwene wake kapena mchemwali wake, aliyense wa iwo adzapeza gawo limodzi m’magawo asanu ndi limodzi, ndipo ngati adali ambiri koposa apo adzagawana gawo limodzi la magawo atatu pambuyo popereka zimene analonjeza kapena kubwezera ngongole mosabweretsa mavuto. Limeneli ndi lamulo lochokera kwa Mulungu, Mulungu ndi wodziwa ndi woleza mtima

❮ Previous Next ❯

ترجمة: ولكم نصف ما ترك أزواجكم إن لم يكن لهن ولد فإن كان, باللغة نيانجا

﴿ولكم نصف ما ترك أزواجكم إن لم يكن لهن ولد فإن كان﴾ [النِّسَاء: 12]

Khaled Ibrahim Betala
“Inunso mupata gawo limodzi mwa magawo awiri (/2) achuma chimene akazi anu asiya ngati alibe mwana (kapena mdzukulu), ngati asiya mwana ndiye kuti inu mupata gawo limodzi m’magawo anayi (1/4) achuma chosiidwacho mutachotsapo zomwe adalamula kuti zipite kwakutikwakuti kapena ngongole zake, naonso akazi anu apata gawo limodzi m’magawo anayi (1/4) pa chuma chomwe mwasiya, ngati mulibe mwana (ndi mdzukulu). Koma ngati mwasiya mwana (ndi mdzukulu), (akaziwo) apata gawo limodzi m’magawo asanu ndi atatu (1/8) pa chuma chomwe mwasiya mutachotsapo chomwe mudanena kuti chipite kwakutikwakuti kapena kulipira ngongole (zanu). Ngati mwamuna kapena mkazi alowedwa m’malo pachuma pomwe alibe mwana (ndi mdzukulu) ngakhale makolo awiri, koma ali naye m’bale wake (wakuchikazi) kapena mlongo wake (wakuchikazinso) aliyense wa iwo apata gawo limodzi m’magawo asanu ndi limodzi (1/6). Ndipo ngati ali ochulukirapo, ndiye kuti agawirana gawo limodzi m’magawo atatu (1/3) a chumacho pambuyo pochotsapo chomwe chidanenedwa kuti chipita kwakutikwakuti kapena kulipira ngongole, popanda kupereka mavuto. Awa ndi malamulo ofunika omwe achokera kwa Allah. Ndipo Allah Ngodziwa kwambiri (pokhazikitsa malamulo); Woleza (pa akapolo Ake)
❮ Previous Next ❯

Verse in more languages

Transliteration Bangla Bosnian German English Persian French Hindi Indonesian Kazakh Dutch Russian Spanish Turkish Urdu Uzbek