×

Ndipo chitantha chisoni, adakutsitsirani mtendere kuti udze pa inu. Ndipo tulo tidagwira 3:154 Chichewa translation

Quran infoChichewaSurah al-‘Imran ⮕ (3:154) ayat 154 in Chichewa

3:154 Surah al-‘Imran ayat 154 in Chichewa (نيانجا)

Quran with Chichewa translation - Surah al-‘Imran ayat 154 - آل عِمران - Page - Juz 4

﴿ثُمَّ أَنزَلَ عَلَيۡكُم مِّنۢ بَعۡدِ ٱلۡغَمِّ أَمَنَةٗ نُّعَاسٗا يَغۡشَىٰ طَآئِفَةٗ مِّنكُمۡۖ وَطَآئِفَةٞ قَدۡ أَهَمَّتۡهُمۡ أَنفُسُهُمۡ يَظُنُّونَ بِٱللَّهِ غَيۡرَ ٱلۡحَقِّ ظَنَّ ٱلۡجَٰهِلِيَّةِۖ يَقُولُونَ هَل لَّنَا مِنَ ٱلۡأَمۡرِ مِن شَيۡءٖۗ قُلۡ إِنَّ ٱلۡأَمۡرَ كُلَّهُۥ لِلَّهِۗ يُخۡفُونَ فِيٓ أَنفُسِهِم مَّا لَا يُبۡدُونَ لَكَۖ يَقُولُونَ لَوۡ كَانَ لَنَا مِنَ ٱلۡأَمۡرِ شَيۡءٞ مَّا قُتِلۡنَا هَٰهُنَاۗ قُل لَّوۡ كُنتُمۡ فِي بُيُوتِكُمۡ لَبَرَزَ ٱلَّذِينَ كُتِبَ عَلَيۡهِمُ ٱلۡقَتۡلُ إِلَىٰ مَضَاجِعِهِمۡۖ وَلِيَبۡتَلِيَ ٱللَّهُ مَا فِي صُدُورِكُمۡ وَلِيُمَحِّصَ مَا فِي قُلُوبِكُمۡۚ وَٱللَّهُ عَلِيمُۢ بِذَاتِ ٱلصُّدُورِ ﴾
[آل عِمران: 154]

Ndipo chitantha chisoni, adakutsitsirani mtendere kuti udze pa inu. Ndipo tulo tidagwira ena a inu pamene ena adangogona kumavutika m’maganizo, chifukwa cha zilakolako zawo, kuganiza mosalungama ndikukhala ndi maganizo a umbuli okhudza Mulungu. Iwo adafunsa: “Kodi ife tili ndi chonena pankhani iyi?” Nena: “Zonse zili m’manja mwa Mulungu.” Iwo amabisa m’mitima mwawo zinthu zimene safuna kuulula kwa iwe. Iwo amanena kuti: “Tikadakhala kuti tidaloledwa kunenapo maganizo athu pankhaniyi, ife sitikanaphedwa pano.” Nena: “Ngakhale inu mukadakhala kunyumba zanu ndithudi ena amene adalembedwa kuti aphedwe akadapita ku malo kumene akadakaphedwa.” Ndipo Mulungu adachita zimenezi kuti ayese zimene zili m’mitima mwanu ndi kuyeretsa zimene zili m’mitima mwanu ndipo ndithudi Mulungu akudziwa zimene zili m’mitima

❮ Previous Next ❯

ترجمة: ثم أنـزل عليكم من بعد الغم أمنة نعاسا يغشى طائفة منكم وطائفة, باللغة نيانجا

﴿ثم أنـزل عليكم من بعد الغم أمنة نعاسا يغشى طائفة منكم وطائفة﴾ [آل عِمران: 154]

Khaled Ibrahim Betala
“Kenako pambuyo pa kudandaula, adakutsitsirani mpumulo - tulo tomwe tidaphimba gulu lina mwa inu. Padali gulu lina lomwe maganizo awo adawatangwanitsa namuganizira Allah ndizoganizira zopanda choonadi, zoganizira zaumbuli; ankati: “Ha! Kodi tili ndi chiyani ife pa chinthu ichi?” Nena: “Zinthu zonse nza Allah.” Akubisa m’mitima mwawo zomwe sakuzionetsa kwa iwe. Akunena: “Tidakakhala ndi chilichonse pa chinthu ichi, sitikadaphedwa apa.” Nena: “Ngakhale mukadakhala m’nyumba zanu, ndithudi kwa iwo amene imfa idalembedwa (kuti amwalire) akadapita kumalo omwalilirawo, koma Allah (adachita izi) kuti awonetse poyera zomwe zili m’zifuwa zanu. Ndikuyeretsa zomwe zili m’mitima mwanu. Ndipo Allah Ngodziwa za mzifuwa.”
❮ Previous Next ❯

Verse in more languages

Transliteration Bangla Bosnian German English Persian French Hindi Indonesian Kazakh Dutch Russian Spanish Turkish Urdu Uzbek