×

Anthu otsatira a m’Buku akukufunsa iwe kuti uwatsitsire buku kuchokera kumwamba. Ndithudi 4:153 Chichewa translation

Quran infoChichewaSurah An-Nisa’ ⮕ (4:153) ayat 153 in Chichewa

4:153 Surah An-Nisa’ ayat 153 in Chichewa (نيانجا)

Quran with Chichewa translation - Surah An-Nisa’ ayat 153 - النِّسَاء - Page - Juz 6

﴿يَسۡـَٔلُكَ أَهۡلُ ٱلۡكِتَٰبِ أَن تُنَزِّلَ عَلَيۡهِمۡ كِتَٰبٗا مِّنَ ٱلسَّمَآءِۚ فَقَدۡ سَأَلُواْ مُوسَىٰٓ أَكۡبَرَ مِن ذَٰلِكَ فَقَالُوٓاْ أَرِنَا ٱللَّهَ جَهۡرَةٗ فَأَخَذَتۡهُمُ ٱلصَّٰعِقَةُ بِظُلۡمِهِمۡۚ ثُمَّ ٱتَّخَذُواْ ٱلۡعِجۡلَ مِنۢ بَعۡدِ مَا جَآءَتۡهُمُ ٱلۡبَيِّنَٰتُ فَعَفَوۡنَا عَن ذَٰلِكَۚ وَءَاتَيۡنَا مُوسَىٰ سُلۡطَٰنٗا مُّبِينٗا ﴾
[النِّسَاء: 153]

Anthu otsatira a m’Buku akukufunsa iwe kuti uwatsitsire buku kuchokera kumwamba. Ndithudi iwo adafunsa Mose zazikulu kuposa zimenezi pamene iwo adati: “Tionetse Mulungu poyera.” Koma iwo anakanthidwa ndi mphenzi chifukwa cha uchimo wawo. Ndipo iwo adapembedza mwana wa ng’ombe ngakhale analandira zizindikiro zathu. Komabe Ife tidawakhululukira zimenezo. Ndipo tidampatsa Mose mphamvu zooneka

❮ Previous Next ❯

ترجمة: يسألك أهل الكتاب أن تنـزل عليهم كتابا من السماء فقد سألوا موسى, باللغة نيانجا

﴿يسألك أهل الكتاب أن تنـزل عليهم كتابا من السماء فقد سألوا موسى﴾ [النِّسَاء: 153]

Khaled Ibrahim Betala
“Anthu amene adapatsidwa buku (Ayuda) akukupempha (iwe Mtumiki) kuti uwatsitsire buku kuchokera kumwamba. Ndithudi, adampemphanso Mûsa zazikulu kuposa zimenezi pomwe adati: “Tiwonetse Allah poyera.” Choncho udawagwira moto wamphenzi chifukwa cha kuipitsa kwao (motowo udachotsa miyoyo yawo chifukwa cha kusakhulupirira kwawo. Zitatero Allah adawapatsa moyo kachiwiri). Kenako iwo adapanga thole (mwana wang’ombe monga mulungu wawo) pambuyo powafikira chisonyezo choonekera. Koma tidawakhululukira zimenezo, ndipo tidampatsa Mûsa chisonyezo choonekera poyera
❮ Previous Next ❯

Verse in more languages

Transliteration Bangla Bosnian German English Persian French Hindi Indonesian Kazakh Dutch Russian Spanish Turkish Urdu Uzbek