| وَيْلٌ لِّلْمُطَفِّفِينَ (1) Tsoka kwa iwo onse amene amagulitsa malonda awo monyenga
 | 
| الَّذِينَ إِذَا اكْتَالُوا عَلَى النَّاسِ يَسْتَوْفُونَ (2) Iwo amene amati ena akamawayesera zinthu amafuna kuti zikwanire muyeso wake
 | 
| وَإِذَا كَالُوهُمْ أَو وَّزَنُوهُمْ يُخْسِرُونَ (3) Koma pamene iwo ayesa kapena awayesera anthu ena amawanyenga
 | 
| أَلَا يَظُنُّ أُولَٰئِكَ أَنَّهُم مَّبْعُوثُونَ (4) Kodi iwo saganiza kuti adzaukitsidwa kwa akufa
 | 
| لِيَوْمٍ عَظِيمٍ (5) Patsiku lalikulu
 | 
| يَوْمَ يَقُومُ النَّاسُ لِرَبِّ الْعَالَمِينَ (6) Tsiku limene anthu a mitundu yonse adzaima pamaso pa Ambuye wa zolengedwa zonse
 | 
| كَلَّا إِنَّ كِتَابَ الْفُجَّارِ لَفِي سِجِّينٍ (7) Iyayi! Ndithudi chiwerengero cha anthu onse oipa chili mu Sijjin
 | 
| وَمَا أَدْرَاكَ مَا سِجِّينٌ (8) Kodi udzadziwa bwanji Sijjin ndi chiyani
 | 
| كِتَابٌ مَّرْقُومٌ (9) Ili ndi Buku lolembedwa
 | 
| وَيْلٌ يَوْمَئِذٍ لِّلْمُكَذِّبِينَ (10) Tsoka pa tsikuli kwa anthu osakhulupirira
 | 
| الَّذِينَ يُكَذِّبُونَ بِيَوْمِ الدِّينِ (11) Iwo amene amakana kuti kuli tsiku lachiweruzo
 | 
| وَمَا يُكَذِّبُ بِهِ إِلَّا كُلُّ مُعْتَدٍ أَثِيمٍ (12) Palibe wina amene amalikana tsikuli kupatula munthu wogona m’machimo
 | 
| إِذَا تُتْلَىٰ عَلَيْهِ آيَاتُنَا قَالَ أَسَاطِيرُ الْأَوَّلِينَ (13) Pamene chivumbulutso chathu chinenedwa kwa iye, iye amati: “Izi ndizo nthano za anthu akale.”
 | 
| كَلَّا ۖ بَلْ ۜ رَانَ عَلَىٰ قُلُوبِهِم مَّا كَانُوا يَكْسِبُونَ (14) Iyayi! Koma m’mitima mwawo ndi mokutidwa ndi zintchito zimene amachita
 | 
| كَلَّا إِنَّهُمْ عَن رَّبِّهِمْ يَوْمَئِذٍ لَّمَحْجُوبُونَ (15) Iyayi! Ndithudi iwo sadzaloledwa kuona Ambuye wawo pa tsikuli
 | 
| ثُمَّ إِنَّهُمْ لَصَالُو الْجَحِيمِ (16) Ndipo iwo adzalowa ndi kulawa moto ku Gahena
 | 
| ثُمَّ يُقَالُ هَٰذَا الَّذِي كُنتُم بِهِ تُكَذِّبُونَ (17) Ndipo kudzanenedwa kwa iwo kuti: “Chimenechi ndicho chilango chija munkachinena kuti sichidzakhalako.”
 | 
| كَلَّا إِنَّ كِتَابَ الْأَبْرَارِ لَفِي عِلِّيِّينَ (18) Iyayi! Ndithudi chiwerengero cha anthu olungama chimasungidwa mu Illiyyun
 | 
| وَمَا أَدْرَاكَ مَا عِلِّيُّونَ (19) Kodi mudzadziwa bwanji kuti Illiyin wapamwambayo ndi chiyani
 | 
| كِتَابٌ مَّرْقُومٌ (20) Ndi Al Mutaffifin	645 Buku lochita kulembedwa
 | 
| يَشْهَدُهُ الْمُقَرَّبُونَ (21) Limene limaonedwa ndi iwo okhawo amene ali kufupi ndi zofuna za Mulungu
 | 
| إِنَّ الْأَبْرَارَ لَفِي نَعِيمٍ (22) Ndithudi anthu onse olungama adzakhala ku malo a mtendere
 | 
| عَلَى الْأَرَائِكِ يَنظُرُونَ (23) Atakhala pa mipando ya wofowofo ndipo ali kuyang’ana uku ndi uku
 | 
| تَعْرِفُ فِي وُجُوهِهِمْ نَضْرَةَ النَّعِيمِ (24) Ndipo udzaona chisangalalo pa nkhope zawo
 | 
| يُسْقَوْنَ مِن رَّحِيقٍ مَّخْتُومٍ (25) Iwo adzapatsidwa kuti amwe vinyo weniweni amene sanatsegulidwepo
 | 
| خِتَامُهُ مِسْكٌ ۚ وَفِي ذَٰلِكَ فَلْيَتَنَافَسِ الْمُتَنَافِسُونَ (26) Womaliza wake adzakhala ndi fungo labwino ndipo pachifukwa cha ichi, aleke onse amene afuna kulimbikira kuti alimbike
 | 
| وَمِزَاجُهُ مِن تَسْنِيمٍ (27) Wosakanizidwa ndi madzi a Tasnim
 | 
| عَيْنًا يَشْرَبُ بِهَا الْمُقَرَّبُونَ (28) Kasupe amene anthu odala adzakhala ali kumwa
 | 
| إِنَّ الَّذِينَ أَجْرَمُوا كَانُوا مِنَ الَّذِينَ آمَنُوا يَضْحَكُونَ (29) Ndithudi! Anthu amene amachita zoipa, anali kuwaseka anthu amene anakhulupirira
 | 
| وَإِذَا مَرُّوا بِهِمْ يَتَغَامَزُونَ (30) Ndi kumacheulana iwo akamadutsa pakati pawo
 | 
| وَإِذَا انقَلَبُوا إِلَىٰ أَهْلِهِمُ انقَلَبُوا فَكِهِينَ (31) Ndipo iwo amati akabwerera kwa anthu awo amabwera ali kunyoza
 | 
| وَإِذَا رَأَوْهُمْ قَالُوا إِنَّ هَٰؤُلَاءِ لَضَالُّونَ (32) Ndipo amati akawaona iwo amati: “Ndithudi awa ndiwo anthu osochera.”
 | 
| وَمَا أُرْسِلُوا عَلَيْهِمْ حَافِظِينَ (33) Pamene iwo sadalamulidwe kuti akhale owayang’anira
 | 
| فَالْيَوْمَ الَّذِينَ آمَنُوا مِنَ الْكُفَّارِ يَضْحَكُونَ (34) Koma pa tsikuli anthu okhulupirira adzaseka anthu osakhulupirira
 | 
| عَلَى الْأَرَائِكِ يَنظُرُونَ (35) Ali pa mipando yawofowofo ndi kumayang’ana
 | 
| هَلْ ثُوِّبَ الْكُفَّارُ مَا كَانُوا يَفْعَلُونَ (36) Kodi anthu osakhulupirira, sanalipidwe mphotho yawo molingana ndi ntchito zawo
 |