| هَلْ أَتَاكَ حَدِيثُ الْغَاشِيَةِ (1) Kodi wamva za chinthu chachikulu chimene chili nkudza
 | 
| وُجُوهٌ يَوْمَئِذٍ خَاشِعَةٌ (2) Nkhope zina, patsiku limeneli, zidzachititsidwa manyazi
 | 
| عَامِلَةٌ نَّاصِبَةٌ (3) Pogwira ntchito zotopetsa
 | 
| تَصْلَىٰ نَارًا حَامِيَةً (4) Iwo adzalowa kumoto woyaka
 | 
| تُسْقَىٰ مِنْ عَيْنٍ آنِيَةٍ (5) Iwo adzapatsidwa madzi oti amwe kuchokera kuchitsime cha moto
 | 
| لَّيْسَ لَهُمْ طَعَامٌ إِلَّا مِن ضَرِيعٍ (6) Sadzakhala ndi chakudya china koma chiphe cha mtengo waminga
 | 
| لَّا يُسْمِنُ وَلَا يُغْنِي مِن جُوعٍ (7) Chimene sichidzawapatsa thanzi kapena kuthetsa njala
 | 
| وُجُوهٌ يَوْمَئِذٍ نَّاعِمَةٌ (8) Nkhope zina, pa tsikuli, zidzakhala zosangalala
 | 
| لِّسَعْيِهَا رَاضِيَةٌ (9) Adzakondwa chifukwa cha ntchito zawo
 | 
| فِي جَنَّةٍ عَالِيَةٍ (10) Atakhala m’minda ya pamwamba
 | 
| لَّا تَسْمَعُ فِيهَا لَاغِيَةً (11) Kumene iwo sadzamva zoononga kapena za bodza
 | 
| فِيهَا عَيْنٌ جَارِيَةٌ (12) Mudzakhala kasupe wa madzi oyenda
 | 
| فِيهَا سُرُرٌ مَّرْفُوعَةٌ (13) Ndi mipando yonyamuka ya wofowofo
 | 
| وَأَكْوَابٌ مَّوْضُوعَةٌ (14) Ndi zikho zomwera zitaikidwa pambali pake
 | 
| وَنَمَارِقُ مَصْفُوفَةٌ (15) Ndi makushoni yoikidwa m’mizere
 | 
| وَزَرَابِيُّ مَبْثُوثَةٌ (16) Ndi mikeka yoyalidwa bwino pansi pake
 | 
| أَفَلَا يَنظُرُونَ إِلَى الْإِبِلِ كَيْفَ خُلِقَتْ (17) Kodi iwo saona mmene ngamira zidalengedwera
 | 
| وَإِلَى السَّمَاءِ كَيْفَ رُفِعَتْ (18) Ndi Kumwamba mmene kudakwezedwera
 | 
| وَإِلَى الْجِبَالِ كَيْفَ نُصِبَتْ (19) Ndi mapiri mmene adalengedwera mokhazikika
 | 
| وَإِلَى الْأَرْضِ كَيْفَ سُطِحَتْ (20) Ndi dziko mmene adalitambasulira
 | 
| فَذَكِّرْ إِنَّمَا أَنتَ مُذَكِّرٌ (21) Motero akumbutse, chifukwa udindo wako ndi wowakumbutsa
 | 
| لَّسْتَ عَلَيْهِم بِمُصَيْطِرٍ (22) Iwe sindiwe munthu wowakakamiza ayi
 | 
| إِلَّا مَن تَوَلَّىٰ وَكَفَرَ (23) Kupatula iye Al Fajr	651 amene abwerera m’mbuyo ndi kuyamba kusakhulupirira
 | 
| فَيُعَذِّبُهُ اللَّهُ الْعَذَابَ الْأَكْبَرَ (24) Motero Mulungu adzamulanga chilango chachikulu
 | 
| إِنَّ إِلَيْنَا إِيَابَهُمْ (25) Ndithudi onse adzabwerera kwa Ife
 | 
| ثُمَّ إِنَّ عَلَيْنَا حِسَابَهُم (26) Ndipo, ndithudi, chiwerengero cha zochita zawo chidzakhala kwa Ife
 |